Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 249
Miyambi ya Patsokwe
Wadzoladzola matope, kumunda kulibe ndime.
-Mawuwa amanena za munthu waulesi amene amayerekezera
kuti walima koma asanalime, kungodzola matope kuti azioneka
ngati amalima.
Wafa atamva.
-Mawuwa amanenedwa zikakhala kuti munthu wina wakumana
ndi mavuto chifukwa chosamva.
Wafa chona, khoswe akondwe.
-Mawuwa amanenedwa anthu akamasangalala kuti munthu
amene amavuta pamudzi wachoka, kapena wamwalira moti
azikhalano mwamtendere.
Wafa mphaka makoswe asangalale.
-Mawuwa amanenedwa anthu akamasangalala kuti munthu
amene amavuta pamudzi wachoka, kapena wamwalira moti
azikhalano mwamtendere.
Wafa ndi dama lake.
-Pa Chichewa mawu akuti dama amatanthauza kunyada, anga-
tanthauzenso kuchita chiwerewere. Ndiye mawuwa amatan-
thauza kuti munthu wafa chifukwa cha kusamva kwake.
Wafulumira kumeza asanatafune, ndiye cham’thimba pakhosi.
-Tisamafulumire kuchita zinthu. Kuchita zinthu modekha n’ko-
funika.
Wafulumira kumeza kutafuna kukadakoma.
-Tisamafulumire kuchita zinthu.
Wagenda katauluka.
-Kulephera kapena kunena mawu zinthu zitapita.
Wakoka chingwe msampha uli pambuyo.
-Mawuwa amanenedwa ngati munthu wapalamula chifukwa
chosamvetsetsa kapena kusaonetsetsa bwino. Ngati munthu
248