Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 248

Miyambi ya Patsokwe n’kumuchitira chipongwe balalo lisanapole. Tisamanyoze kapena kuchitira chipongwe anthu amene akutithandiza. Wachikumbakumba wasiya dzenje, kumudzi usakati “ndiwo!” -Mawuwa amanena za munthu yemwe wapita kukafuna mbewa ndiye wakumba n’kutopa n’kusiya una, ndiye kupita kunyumba n’kumakadandaula kuti alibe ndiwo. Mwambiwu umagwiritsid- wa ntchito ngati anthu akambirana zinazake ndiye akuuzana kuti asakaulule zinthu zimene amakambiranazo. Wachita mwa mlatho. -Kuchita chinthu chinachake kuti upulumuke ngakhale kuti sumafuna kuchichita. Wachoka pa Chivuulandiwo wafika pa Chimwamchere. -Mawuwa amanena za munthu amene anali woipa kale ndiye waipiratu. Wada m’mimba, akanakhala maso tikadatsukamo. -Mwambi uwu umanenedwa zinthu zikavuta kwambiri moti palibe chimene mungachite. Wadabwa chule m’madzi muli mwake. -Mawuwa amanenedwa ngati munthu wadabwa ndi zinazake chifukwa choti si mmene zimayendera nthawi zonse. Waduka lende, ana asewera pansi. -Mawuwa amanenedwa ngati munthu wamwalira n’kusiya ana. Wadula mchira. -Mawuwa amanenedwa ngati munthu wina wapalamula kapena wachita chinachake choipa. Mawu amenewa anachokera ku zimene mchira wa buluzi umachita ukaduka. Wadyera amakumba manda ake ndi mano. -Dyera limaphetsa. Munthu akhoza kudwala matenda osiyana- siyana chifukwa choti amadya kwambiri. 247