Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 244

Miyambi ya Patsokwe Usamasule mtolo chifukwa muli liwiro la tonse. -Munthu usanapute mlandu ndi bwino kumaganizira kuti zochi- ta zakozo zikhudzanso anthu onse a m’banja lako. Usamaswere dzungu m’lichero. -Kuswera dzungu m’lichero kukungotanthauza kusaugwira mti- ma. Ukamva nkhani yachilendo si bwino kuyamba kufotokozera anthu chifukwa ukhoza kupezeka ukufalitsa mabodza. Usamatame ntchito zake mtima wake usanaudziwe. -Osamafulumira kuweruza munthu pa ntchito zake usanamudziwe bwinobwino. Usamathawe mkamwa, kumene ukupitakonso ukalipeza. -Padziko lapansili anthu ambiri ndi am’kamwa moti palibe ku- mene ungalowere osakapeza anthu otero. Usamati ndathawa mlomo, kumene ukupitako ukaupeza. -Kuthawa mlomo ndi kuthawa kulongolola. Mavuto ali ponseponse ndipo sitingawathawe. Amene akufuna kuwathawa kuli bwino angomwalira. Usamati ndi chilonda, lidzakula. -Mwana akalakwitsa ndi bwino kumulangiza m’malo mongo- mulekerera. Kuti mwana akule bwino tiyenera kuyamba kumu- langiza ali wamng’ono. Apo ayi chilonda chidzasanduka bala lalikulu khalidwe lake litafika poipa. Usanalavule mawu, yamba wawalawa kaye. -Ndi bwino kumaonetsetsa kuti zimene tikunena ndi zoona ko- manso zabwino, zomwe sizingakhumudwitse ena. Usanamwaze nthenga, kumayamba waona kaye ngati un- gazitolele. -Kunena mabodza kuli ngati kumwaza nthenga. Nthenga zim- apita ndi mphepo. Ndiye usananene bodza ndi bwino 243