Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 243

Miyambi ya Patsokwe Usakhulupirire mazira a Koka. -Mbalame ya Koka imafuna malo omwe Khwangwala waikira kale mazira ake n’kumuthamangitsa kuti aikirepo ake. Choncho, munthu sangadziwe dzira lomwe litulutse ana a Koka kapena a Khwangwala. Mwambiwu umatanthauza kuti zam’tsongolo siz- idziwika. Usakonde vembe, koma ukonde chulu. -Ukakwatira umakhala wakwatira mudzi wonse. Usamangokon- da mkazi wako yekhayo komanso makolo ake. Usalimbitse goli pomanga bulu wako. -Pofufuza zinazake timafunika anthu kuwatenga pang’onopang’ono kuti asachite mantha koma akhale omasuka. Usamadikire kuti madzi afike m’nkhosi. -Usamadikire kuti vuto liipe kwambiri ndiye n’kumayamba ku- chitapo kanthu. Usamakokomeze chisanu ngati chitolankhuni. -Munthu akasauka asamangodandaula, koma azigwira ntchito kuti umphawiwo umuchoke. Usamaloze chitsa usanachibzole. -Osamachenjeza anzako kapena kuwauza kuti asiye kuchita zoipa zinazake zomwe iwenso umachita. Usamanyoze thewera mkuzi uli nawo. -Usamanyoze mkamwini wako pamene mwana wako adakali nayebe. Usamapake mnzako chipwidza. -Mawuwa amanenedwa pouza munthu kuti asamanamizire mnzake. Chipwidza ndi ndowe kapena matudzi a chiweto. 242