Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 242

Miyambi ya Patsokwe Umavomera ngati womva (wodwala) dzino. -Mawuwa amatanthauza kuvomera mokaikira, moti wina san- gagwire chenicheni. Munthu amafunika kunena motsimikiza osati mokayikira. Umayambira madzi akadali m’mapazi. -Vuto likamayamba kumene limakhala losavuta kuthana nalo monga matenda, njala ndi zina. Umayambirira madzi asanafike m’maondo. -Vuto likamayamba kumene limakhala losavuta kuthana nalo monga matenda, njala ndi zina. Umayambiza madzi ali m’maondo. -Vuto likamayamba kumene limakhala losavuta kuthana nalo monga matenda, njala ndi zina. Umazika mzimbi woyera kumene wachoka ndi kumene upita. -Kulikonse kumene wachoka ndi kumene ukupita ndi bwino kusiya mbiri yabwino kuti anthu adzakulandirenso mawa. Mzimbi yoyera ndi nthenga yoyera, yomwe ikuimira mbiri yabwino. Umphawi n’kulumpha chiunda. -Munthu ukachoka kwanu umasowa zambiri zimene unkazipe- za kwanu. Anthu amavutika akakhala koyenda. Unjiunji ajiwitsa. -Kukondetsa zinthu kumabweretsa mavuto makamaka zinthuzo zikakhala zoipa. Unyinji ukoma, uipira kutha mchere. -Kuchulukana n’kwabwino, kumangoipira kuti zinthu siz- ichedwa kutha. Koma pakakhala ntchito imayenda ndithu. 241