Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 240

Miyambi ya Patsokwe unamuuza kuti, “Musachite mantha achimwene. Panotu ta- kumana amuna okhaokha. Kaya inu mukuchokera kuti ulen- dowu?” Poyankha munthu uja anati: “Ine ndikuchokera m’malunjemu ndimakasaka.” Ndiyeno mkango unati, “Popeza tonse tikuchokera kosaka, aliyense asaulule mnzake. Ulenje umasimba wako, osati wamnzako.” Atangosiyana pamenepo, mkango uja unalowa m’tchire ndipo munthuyo anathamangira kwawo ali ndi mantha. Kenako anayamba kuuza anthu kuti wa- kumana ndi mkango utagwira nyama. Mkango uja utamva zim- enezi, unapita kunyumba kwa amfumu n’kukagwira mwana wawo n’kumupha. Kenako unakamuika m’nyumba mwa mlenje uja. M’mudzimo munayambika chipwirikiti chifukwa cha kusowa kwa mwanayo ndipo mfumu inalamula kuti anthu afufuze amene watenga mwana wakeyo. Atafufuza anapeza mwanayo atafa koma ali m’nyumba mwa mlenje uja ndipo mfu- mu inalamula kuti nayenso aphedwe. Ulesi ndi matenda. -Ukalekerera ulesi chimakhala chizolowezi ndipo chimasanduka matenda. Ulesi ulibe mtolo. -Ulesi umabweretsa njala komanso mavuto ena. Munthu waulesi sangakhale ndi kanthu kolozeka. Ulumbwana ulibe mainja awiri. -Mawuwa amatanthauza kuti munthu sangakhale mwana n’kupezeka kuti wakhalapo mudzi wina n’kusamuka, kenako n’kubwereranso kubwinja loyamba lija. Mwambiwu umatan- thauza kuti munthu akamakula amafunika kusiya chibwana. Munthu akakhala mwana nthawi zambiri sachita zinthu mozindikira. 239