Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 24

Miyambi ya Patsokwe n’kuyamba kumuchitira zoipa. Ndi bwino kumangoyamikira chifukwa sudziwa chidzachitike mawa. Mwina mwayi udzakha- la wako. Chakubala chimasanzitsa, obereka amanyansidwa. -Makolo ayenera kukhutira ndi mphatso za ana omwe Mulungu wawapatsa. Chakudya chawekha sichikoma, koma cholimbirana. -Pali zinthu zina zomwe sizikoma kupanga wekha monga map- wando, ntchito komanso zina. Ndi bwino kumagawanako ndi ena zimene tili nazo. Chakudya chimodzimodzi sichinona. -Ndi bwino kumasinthasinthako pochita zinthu. Chakudya chimodzimodzi sichinonetsa. -Si nzeru munthu kukhulupirira nzeru zake zokha. Ndi bwino kumafunsako ena kuti tikhale ndi chinthunzithunzi chokwanira cha moyo kapena ntchito. Chakudya sichichepa, chimachepa ndi chovala. -Chovala chimodzi simungathe kuvala anthu awiri nthawi imodzi. Koma chakudya ngakhale chitachepa bwanji mukhoza kugawana. Mawuwa amanenedwa poitanira ena kuti adzadye nawo chakudya. Kumayamikira zimene timapeza. Chakudza sichiimba ng’oma. -Kumakonzekera zam’tsogolo, chifukwa zamawa sizidziwika. Chakufa sichiopa kutulutsa fungo. -Chilichonse chimakhala ndi zotsatira zake ndipo sitingaziletse. Munthu amene walakwa walakwa basi. Mbiri yake imaipa ndipo amapatsidwa chilango. Chakufa sichiyankhula. -Munthu amene kunalibe sangaikire umboni pa nkhani imene 23