Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 235

Miyambi ya Patsokwe anapezako anzake amene anali atakhala kwa nthawi yaitali ndi bwanayo. Anzakewo anali ndi zinthu zambiri zimene anapata pa zaka zimene anakhala akugwira ntchito. Chifukwa chosirira kukhala ndi katundu ngati wa anzakeyo ndiponso kukhala wolemera, anaganiza zoti apeze mankhwala. Mumtima anagani- za kuti mankhwalawo amuthandiza kuti bwana wake azi- mukonda, kuti iye akhupuke ndiponso kuti bwanayo achotse ena mwa anzake ena amene sankagwirizana nawo. Ngati zime- nezi zikanatheka ndiye kuti iye akanalandira udindo ndiponso akanamuwonjera malipiro ake. Atapita kwa sing’anga anapezadi mankhwala amene ankafunawo. Sing’anga uja popereka mankhwalawo anamuuzitsa kuti asakagone kwa masiku atatu chifukwa ngati angakagone ndiye kuti akatupa mimba. Koma tulo ndi nkhondo timagoneka olira. Tsiku loyamba analimbadi m’maso osagona. Pamene kunkacha tsiku lachiwiri tulo tinali ti- tasonkhana, moti amati akati aimirire sizimatheka. Atakhala pansi kuyambika kwa matenda kunali komweko. Anzake amene ankafuna kuwalodza aja atamufunsa anafokotokoza kuti, “Pepani anzanga, munthune ndimafuna kulemera. Ndiye mankhwala amene ndinapeza, chizimba chake china n’choti ndisagone masiku atatu, koma ndalephera kuchikwaniritsa. Motero thamangani mukamuuze sing’anga wandipatsa mankhwalawa kuti atsukule nyangayo n’cholinga choti ine ndikhale ndi moyo.” Anzake aja atapita anakapeza kuti sing’anga uja anali atamwalira cha dzana lake moti anthu anali asanachoke pasiwa. Anzake atabwerako anamufotokozera mmene ayendera. Chifukwa chodziwa kuti kwake kwatha anayamba kulira ndipo polirapo anali kulira mochenjeza kuti, “Abale anga munthu ukasauka si nzeru kugwira nyanga, taonani zandichitikira inezi!” Pamenepo anzakewo anavo- merezadi kuti, “Ukasauka usamagwire nyanga.” Nyanga 234