Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 234

Miyambi ya Patsokwe Ukapha tonde wonona, usamathe mawu. -Tisamanyade kapena kudzitama tikakhala ndi chinthu chinachake. Ukapindula wotcha, akazi ndi alendo. -Munthu asamaiwale kapena kunyoza abale ake chifukwa cha mkazi, banja limatha koma chibale sichitha. Ukapita kuthengo usamakhudzane ndi mtuvituvi, ungawonje- zere kununkha. -Osamaloza ena chala chifukwa cha zolakwa zako. Anthu ena akalakwa amayamba kuloza ena zala kuti ndiye alakwitsa kapena achititsa kuti alakwe. Ukaponya chakudya pamadzi, udzachipeza. -Ndi bwino kukhala woolowa manja chifukwa tsiku lina anthu omwe ukuwathandizawo angadzakugwire dzanja. Ukasauka usadzimangilire. -Munthu ukasauka usamadzichitire zoipa, monga kudzikhweza kapena kumwa tameki, chifukwa palibe chomwe ungapindu- lepo. Ukasauka usamagwire nyanga. -Ngati ndife osauka tizivomereza m’malo moyamba kudalira nyanga, kuba kapena kupha anthu. Ukasauka usamaloze anzako chala. -Ukasauka usamanamizire anzako kuti ndiye akupangitsa. Ukasawuka usamagwire nyanga. -Si bwino kumachitira ena nsanje kapena kumawafunira zoipa ukakhala kuti iweyo ulibe kapena sungathe kuchita zinazake. Nkhani yake imati, mkulu wina anakafunsira ntchito kwa bwa- na wolemera kwambiri. Kumene ankagwira ntchitoko 233