Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 233
Miyambi ya Patsokwe
nsima yake.
Ukapalamula uzikhala wokonzeka.
-Munthu ukalakwa umayenera kuyembekezera kuti ukumana
ndi zotsatirapo zake.
Ukapalana ubwenzi ndi mphezi, suopa kung’anima.
-Munthu amene akufunitsitsa chinthu ayenera kukhala wolimba
mtima.
Ukapalana ubwenzi ndi Vumbwe umakhala uli ndi Nkhuku.
-Tizikhala titakonzeka tisanayambe kuchita chilichonse. Kuti an-
thu azikonda kubwera pakhomo umafunika kumawadyetsa
bwino.
Ukapeza ana a olemera akukazinga maso a nkhono, kazinga
nawo.
-Tizichita zimene anzathu akuchita.
Ukapeza anzako akukazinga maso, nawenso kazinga ako.
-Munthu uzichita nawo zomwe eni mudzi akuchita kapena wa-
wapeza akuchita.
Ukapeza anzako akutong’ola maso, nawe tong’ola ako.
-Tizichita zimene anzathu akuchita.
Ukapeza eni mudzi akukazinga maso, nawenso kazinga ako.
-Tizichita zimene anzathu akuchita.
Ukapeza nyamu zikuuluka, ima pambali uzitola
imodziimodzi, upeza zadzaza nsengwa. Koma ukaikapo dzan-
ja, udzatola imodzi yokha.
-Munthu ayenera kumachita zinthu mofatsa kuti apeza zabwino.
Dyera komanso changu nthawi zina sizithandiza.
Ukapha mwiri umabweza mphanda.
-Munthu akalemera amakhala wokongola ngati mwiri. Ndiye
zikatero si bwino kuyamba kunyada n’kumanyoza ena.
232