Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 231

Miyambi ya Patsokwe Ukakwera m’mwamba usamatukwane pansi, ungasowe woku- tola ukatsakamuka. -Si bwino kumanyoza ena ukakhala pabwino chifukwa zik- adzakuvuta udzasowa wokuthandiza. Ukakwera m’mwamba usamatukwane pansi. -Ukakhala pabwino usamanyoze anzako chifukwa zikadzakuvu- ta udzasowa wokuthandiza. Mwachitsanzo, ukamatukwana an- thu omwe ali pansi ukakwera mumtengo, ukatsakamuka umasowa wokutola. Ukakwera pamsana pa njovu, usamati kulibe mame. -Osamachita matama ukakhala pabwino chifukwa za mawa siz- idziwika. Ukakhala pabwino usamanyoze anzako. Ukalakwa usamafulumire kupita kuboma. -Kumayamba watsikiza kuti ndiwe wosalakwa ukamapita ndi nkhani kuboma chifukwa ukhoza kungomangidwa nazo ulele. Ukalemera cheuka, ona chakulemeretsa. -Tisamaiwale anthu amene atithandiza kuti tifike pano. Ukalemera tsekako, ‘kulinji’ akudza m’njira. -Ukalemera usamadzitame chifukwa akuba akhoza kukubera iwe n’kufota. Chakudza sichiimba ng’oma. Ukalemera umayankhulira m’chigulu. -Tikalemera tisamaonetse zonse zomwe tili nazo chifukwa ena akhoza kutibera. Chigulu ndi chikho chomwera mowa. Kuyank- hulira m’chigulu kukusonyeza kuti suima pachulu n’ku- mabwebwetuka za kulemera kwako. Ukalemera usamavinire poyera, koma m’nyumba. -Tikalemera tisamaonetse zonse zomwe tili nazo, chifukwa ena akhoza kutibera. 230