Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 230

Miyambi ya Patsokwe ungadzazifune. Ukakhuta umawotcha nkhokwe. -Tisamapondereze ena powachotsera mwayi wopeza zosowa zawo. Ukakhala pabwino usamataye zinthu chifukwa njala ikho- za kukupwetekanso. Ukakhuta usamatsinkhire anzako ndiwo. -Si bwino kupondereza ena ife tikakhala pabwino. Ukakhuta usamatukwane yemwe wakupatsa chakudya. -Munthu akakhuta amaganiza kuti njala singamupwetekenso. Choncho amayamba kunyoza komanso kuchitira mwano amene amamuthandiza. Tisamachite khalidwe limeneli. Ukakoka dzungu, umakoka ndi ana ake omwe. -Munthu ukakwatira kapena kukwatiwa, osasakonda munthu yekhayo komanso abale ake. Ukakoka khoka, umakokanso zonse zomwe zilimo. -Munthu ukakwatira kapena kukwatiwa osasakonda munthu yekhayo komanso abale ake. Ukakongola kwatiwa, chifukwa kunyansa kumachita kubwera. -Mwayi ukapezeka tiziugwiritsa ntchito. Ukakongola leka thyonyo. -Ukakhala wokongola usamanyoze anzako chifukwa za mawa sizidziwika, mwina ukhoza kudzakhala ndi chilema m’tsogolo. Ukakwatirana ndi nyani chifukwa cha chuma chake, chu- macho chimatha, iwe umatsala ndi nyaniyo. -Ndi bwino kumayang’ana munthu wakhalidwe labwino ukamafuna kukwatira m’malo motsatira chuma chomwe ndi mchira wakhoswe. 229