Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 23

Miyambi ya Patsokwe Chaipira Galu kuluma Mbuzi. -Munthu anganene mawuwa akamadandaula ndi mavuto omwe amulepheretsa kuchita zinthu zimene amafuna. Munthu an- ganenenso mawuwa podandaula zinthu zopanda chilungamo zimene ena amuchitira. Chakanachakana, dazi lilibe mankhwala. -Pali zinthu zina zomwe ndi umunthu wathu sitingazithe. Zote- rezi tiyenera kuvomereza kuti zikhale mmene zilili ndi kukhuti- ra ndi zimene tili nazo. Chakanachakana, Kalulu sasenda nguwo. -Tizivomereza ngati zinthu zavuta, osamachita ukamberembere. Chako n’chako sichilingana n’chamwini. -Chinthu chako umachigwiritsa ntchito mwanjira iliyonse, koma chamwini umachiopa. Chakomera Mbuzi kugunda Galu, Galu akati agundeko akuti wapenga. -Osamachita zinthu mokondera kapena kumachitira ena nkhanza tikudziwa kuti ena atiikira kumbuyo. Chakomera Mbuzi kugunda Galu, Galu akati alumeko akuti waboola nguwo. -Osamachita zinthu mokondera kapena kumachitira ena nkhanza tikudziwa kuti ena atiikira kumbuyo. Chakomera nzako umasimba. -Ndi bwino kumayamikirako zabwino zimene ena achita. Chakometsa Ntchentche, inachilimika kuuluka. -Kuti munthu upeze bwino umafunika kukhala ndi podalira ko- manso kuchita khama. Chakonda mnzako mlekere, mawa chidzakonda iwe. -Mnzathu akachita mwayi si bwino kumuchitira nsanje 22