Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 227

Miyambi ya Patsokwe Uhule ndi mtima. -Munthu sakhala hule chifukwa cha mmene akuonekera koma mtima wake. Ukabwereka miyendo ya munthu, umapita kulikonse kumene iyeyo akufuna. -Munthu amene ali ndi ngongole sakhala ndi ufulu wochita zimene akufuna ndi ndalama yake. Ukachedwa umagula khutu. -Mwambiwu umachenjeza munthu amene amachita zinthu mochedwa kapena mwachidodo. M’malo mogula nyama yabwino amakapena kuti latsala ndi khutu. Ukachenjera sunona. -Nthawi zambiri amene amakonda kuyankhulayankhula kapena ochenjeretsa amakhala opanda nzeru. Chimodzimodzinso okon- gola, amangokongola nkhope koma n’kukhala opanda nzeru kapena opanda khalidwe. Ukachoka usamachitire dziko chipongwe, umakumbukira pokabwera. -Pochoka pamalo umayenera kuchoka mwaulemu kuti mawa adzakulandirenso. Ukachoka usamatseke potulukira ndi mwala koma mayani. -Osamachoka pankhomo utawonongapo chifukwa tsiku lina udzabwerera. Ukadya, umadziwa azungu ndi alendo. -Ukalemera usamanyoze anzako chifukwa ntchito ikatha, sudza- khalanso ndi azungu koma abale ako. Komanso anzako omwe unkawanyoza. Pang’ono mwambiwu umalimbikitsa tsankho. Mukadzaugwiritsa ntchito musadzadabwe apolisi akadza- kumangani. 226