Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 226
Miyambi ya Patsokwe
Udakula bwanji wopanda tsinde?
-Tisamaiwale abale komanso anthu ena omwe atithandiza kuti
tifike pamene tili lero.
Udam’dyeranji pholokoto anzako akudya kawerawera?
-Tizigwira ntchito molimbika kuti tipeze zosowa zathu. Polima
timawerama osati kuimirira.
Udaotha chichiri cha ukonde.
-Chichiri chimathandiza kuti ukonde ukhale wokungika. Mawu-
wa amagwiritsidwa ntchito potanthauza munthu yemwe wapal-
amula kapena kulakwira anthu omuthandiza.
Ufiti ndi mawu.
-Tisamayankhule zonyoza kapena kutukwana chifukwa china
chikachitika anthu amaloza ife.
Ufulu umabweza ufulu.
-Ukachitira anzako zabwino nawonso amakuchitira zabwino.
Ufulu wa ng’ombe wogwedeza mchira.
-Pali anthu ena omwe amati munthu akawachitira zabwino
sathokoza. Monga mmene ng’ombe imachitira akaipatsa
chakudya, chinthu chimene imachita ikamayamikira ndi
kugwedeza mchira, sibweza kalikonse.
Ufumu wanji wa Kadzidzi wokhala pachitsa?
-Mfumu isamangokhala neng’a, koma izichita zinthu zomwe
zingathandize anthu ake.
Ufune kaya uleke, kulidetsa tsitsi ndi ufulu.
-Chilichonse chili ndi nthawi.
Ufunthafuntha mphuku, mbiri nja khoswe.
-Munthu akakhala woipa kapena wochenjeretsa amasowa
mtendere, chifukwa chilichonse choipa amangoti wachita ndiwe.
225