Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 225

Miyambi ya Patsokwe Ubale waufulu uli pamalemba. -Anthu amagwirizana akakhala patali, koma akakhala pamodzi sachedwa kukhulana. Ubwenzi wa “ponda apo mpondepo.” -Chimenechi ndi chikondi chenicheni chochitira zinthu limodzi. Ubwenzi wa galu uli kumchira. -Ubwenzi weniweni uyenera kumakhala ndi ntchito zake, osati kumangonena pakamwa pokha kuti awa ndi anzanga, zika- wavuta n’kuwathawa. Ubwenzi wa madzi ndi nsomba. -Ubwenzi weniweni umakhalapo ngati anthu amakhalira limodzi osasiyana zivute zitani. Ubwenzi wa Nkhwazi woyanjana polira. -Polira pokha ndi pamene Nkhwazi zimagwirizana. Koma ikag- wira nsomba imadya yokha. Mawu amenewa amanena za mun- thu amene amakhala mnzako akavutika, koma zikamamuyen- dera saoneka. Ubwenzi weniweni umaoneka zinthu zikavuta. Ubwenzi wa nsomba wosalekana ndi madzi. -Ubwenzi wa nsomba ndi madzi ndi weniweni. Pamene madzi aphwera nsomba imafa. Mawuwa amatanthauza ubwenzi weni- weni woferana. Ubwino wa dzuwa umaoneka likapita. -Munthu wabwino amadziwika akapita. Mwachitsanzo, ena amazindikira kuti mkazi kapena mwamuna wawo anali wabwino banja likatha. Nthawi zambiri amazindikira zimenezi akakwatirana ndi chilombo. Uchembere n’kudyerana. -Mnzako akukuchitira zabwino nawenso ndi bwino kumuchitira zabwino. 224