Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 223

Miyambi ya Patsokwe Tsoka lilibe fungo. -Tsoka limabwera mwadzidzidzi. Tsoka limayambira kumwendo. -Tsoka limayamba pang’onopang’ono. Anthu ena a ku Africa kuno amakhulupirira kuti munthu akamayenda ndiyeno n’ku- puntha, ndiye kuti kumene akupitako akapezako matenda kapena maliro. Mawuwa amagwiritsidwa ntchito ponena kuti uli ndi tsoka lalikulu. Tsoka limayambira pa kanthu kakang’ono komwe anthu sangakaganizire kuti kangayambitse vuto laliku- lu. Tsoka msinde chimanga chilinda moto. -Mawuwa amatanthauza kuchita tsoka lalikulu. Tsoka n’kusuzumira m’chizombwe. -Munthu wachidwi kwambiri amatha kukumana ndi mavuto. Mwachitsanzo, posuzumira pachulu amatha kulavuliridwa ndi njoka. Tsoka ndi mphwayi, ukafuna kanthu koma kuyesa. -Munthu wamphwayi sangapeze zimene akufuna. Tizichita kha- ma tikamachita zinthu. Tsoka sasimba, koma mwayi. -Ukapulumuka tsoka, si bwino kukakamira khalidwe lomwe lakubweretsera tsokalo chifukwa mwina pambuyo pake ukhoza kutaya moyo wako kapena osapulumukanso. Tsoka silinunkha. -Tsoka limabwera mwadzidzidzi. Tsokonombwe adatha mtunda n’kudumpha. -Nthawi zina ndi bwino kuchita zinthu mosathamanga komanso ndi bwino kulimbikira kuti zomwe ukufuna zitheke. Zinthu 222