Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 222

Miyambi ya Patsokwe Tsoka la mnzako likupatse nzeru. -Wina akalakwitsa chinachake, ndi bwino kumaphunzirapo kan- thu kuti tisabwerezenso zomwezo. Moyo ndi waufupi kwambiri kuti munthu aphunzire pa zolakwa zake zokha. Tsoka la mnzako n’lakonso. -Nthawi zina tsoka la ena limakhudzanso anthu ena, monga oyandikana nawo nyumba. Tizithandiza ena akakhala m’mavuto. Tsoka la msinde, chimanga chilinda moto. -Misinde imacha mwamsanga moti anthu amayamba kuidya chimanga chisanakhwime. Anthu ena amazunza anzawo mosa- samala kanthu kuti ndi abale awo. Tsoka la Nkhuku lopita kumanda nthenga zokha. -Limeneli ndi tsoka lalikulu kwambiri lomwe munthu anga- kumane nalo. Nkhuku ikafa maliro ake saikidwa m’manda. Ku- manda kumangopita nthenga zokha basi. Tsoka la mfutso lobwerera pamoto kawiri. -Limeneli ndi tsoka lalikulu kwambiri lomwe munthu anga- kumane nalo. Tsoka likakuda Kamba amaoneka ngati mwala. -Kamba ngati sakusuntha amaoneka ngati mwala. Nkhani zina zimakhala zosamvetsetseka. Wina akhoza kudwala mwakayaka- ya koma wina wolimba n’kumwalira kusiya wodwalayo. Tsoka likalimba amakuluma ndi galu wako yemwe. -Zinthu zikati zivute, nthawi zina anthu amene umawadalira ndi amene amakutaya. Tsoka likalimba umakuotcha ndi mkute. -Zinthu zikati zivute, nthawi zina anthu amene umawadalira ndi amene amakutaya. 221