Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 221

Miyambi ya Patsokwe Tsatanetsatane ndi njira. -Munthu poyankhula sangathe kunena ndendende zonse zimene waona kapena zimene wina wanena. Tulo ndi nkhondo, tinagonetsa anamalira. -Ena amaganiza kuti, kuti asonyeze kuti amakonda kwambiri m’bale wawo amene wamwalira, afunika kulira usiku onse. Ko- ma tulo tilibe masewera, timatha kugonetsa munthu wotereyu. Tsekera lili pachipadzo. -Udzu wabwino umasadzulidwa ndi nsungwi. Chimodzimodzinso mwana, kuti akule bwino timayenera kuyambiratu kusadza makhalidwe ake oipa adakali wamng’ono. Tsiku limodzi silivunda nyama. -Zinthu zina sizingatheke tsiku limodzi, pamafunika nthawi. Tsiku limodzi siliwoza mbewa. -Nthawi zina ndi bwino kudikira pochita zinthu chifukwa tikachita mofulumira nthawi zina zinthuzo sizichitika bwino. Zinthu zina sizingatheke tsiku limodzi, pamafunika nthawi. Tsiku lofera nyani mitengo yonse imaterera. -Anyani ena ankadalira mitengo kuti agalu akamabwera an- gokwerapo. Koma tsiku lina agalu akubwera anyaniwo anapeza kuti mitengo yonse inali yoterera moti anagwidwa. Tizikonze- kera zinthu zomwe zikhoza kutigwera. Tsitsi likakula udzasowa wokumeta. -Munthu wosamva amamva akakumana ndi mavuto. Tsoka chitambe. -Chitambe chimakhwima nsanga kuposa masamba ena. Zimene- zi zimachititsa kuti chikhale choyambirira kudyedwa. Mwana woyamba ndi amene amakumana ndi zoopsa. Tisamathamangi- re kuchita zinthu tisanaganize bwino. 220