Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 220
Miyambi ya Patsokwe
cha paulendo chifukwa sitikudziwa zimene zingatichitikire.
Tokoma sitichedwa kutha, ndaonera dowe.
-Zinthu zabwino sizichedwa kutha. Tisamaike mtima wathu pa
zinthu zosakhalitsa.
Tokoma sitikuti “leke.”
-Zabwino sizingauze munthu kuti asiye, umafunika wekha kud-
ziwa kuti pamene ndafikapa ndakwana.
Tokoma sitioneka tsiku limodzi.
-Tizifatsa ndi kumaupeza mtima chifukwa zabwino zimabwera
pang’onopang’ono.
Tokoma tidadza n’takalamba.
-Zokoma zimabwera munthu utatha kale kapena nthawi imene
sumayembekezera.
Tonde akadula, sabwerera.
-Tonde akadula cholinga chake chimakhala kupita komwe kuli
matazi. Akawapeza amangoumirira komweko. Chimene mtima
wako watsimikiza osaleka mpaka chitatheka.
Tsabola wakale sawawa.
-Mawuwa amatanthauza kuti malangizo a anthu akale ndi
osathandiza.
Tsachipenembe anaotcha nkhokwe.
-Munthu amene amadziwa bwino mmene zinthu zimakhalira
ndi kuyendera ndi amene nthawi zina amabweretsa chipwirikiti.
Tsamba likagwa manyazi amagwira mtengo.
-Mwana akalakwa manyazi amagwira makolo ake. Makolo
akhoza kupeza mavuto chifukwa cha ana awo.
Tsata mphero.
-Mawuwa amanenedwa pochenjeza munthu kuti angopitira
kukapera ufa, osati kukanena mabodza.
219