Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 218

Miyambi ya Patsokwe Tambala n’tabwali, amamasula tambwali mnzake. -Ukafuna kugwira mbala umafunika kutuma mbala inzake. Tambala salira kwa eni, amalira kwawo. -Munthu sungakhale mfumu kwa eni, koma kwanu. Tangovutika, opanirira mphika ali chete. -Nthawi zambiri anthu amene amagwira ntchito yolemetsa ko- manso yokhetsa thukuta sapeza ndalama zambiri, koma mabwana awo omwe amangokhala muofesi. Tapita m’njira adasiya tonse m’khola. -Tikamadutsa pamudzi wa abale kapena anthu owadziwa tiyenera kumakawaona kuti ali bwanji, chifukwa tikhoza ku- wadutsa iwo ali m’mavuto kapena asakupeza bwino. Tatuma chitsiru kuti chimange mtembo. -Mawuwa amanenedwa anthu akamadandaula kuti munthu amene anamutuma kuti agwire ntchito inayake wailephera kapena wachita zokhumudwitsa. Tentha tizime adapsetsa anzake. -Mawuwa amanena za munthu amene ankauza anzake kuti ayatse moto ndipo auzimitsa pamapeto pake n’kupezeka kuti waotcha anzakewo. Anthu ena amaputira anzawo mavuto chifu- kwa cha khalidwe lawo loipa. Mwachitsanzo, bambo wokonda mowa amachititsa kuti ana ake avutike. Thendo limakoma, nyama kulowa m’mano. -Masamba otendera amakoma. Komabe nyama ndi yokoma kwambiri koma kulowa m’mano. Ukafuna zokoma umafunika kudziwa kuti zili ndi zowawa zake. Thumba la Tambe amamasula ndi Tambe yemweyo. -Munthu akakhala kamberembere amene amadziwa khalidwe lake ndi kamberemberenso. Tambwali akamanga thumba, 217