Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 216

Miyambi ya Patsokwe Sunga khosi, mkanda uwoneka. -Munthu amafunika kupirira komanso kudziletsa kuti adzapeze zabwino m’tsogolo. Suntche adati, “Pita pansi ukamve.” -Osamamvera zilizonse zimene anthu akunena. Kumatsimikizira kaye ngati zilidi zoona. Suzi suzi, alimba ndi mbalame zake. -Munthu ukatchera msampha umasuzumira kuti uone ngati wagwira kanthu. Ndi bwino kumayang’ana kawirikawiri chin- thu chomwe tikuyembekezera. Suzumire adaphetsa mkhalakale. -Mbalame ina yomwe inkhakhala kuphanga sinkasuzumira pan- ja kuopa kuphedwa. Tsiku lina inzake inabwera kudzakhala nayo ndipo mbalameyi inalangiza inzakeyo kuti isamasuzumire panja ikamva phokoso. Koma mbalameyi sinamvere moti inasu- zumira ndipo anthu ataiona anaipha pamodzi ndi inzake ija. Munthu wina akalakwa n’kumafufuzidwa amapezeka kuti ag- widwa ndi ena amene anabisala n’kulangidwira limodzi. Ku- chenjeretsa kapena kusaugwira mtima kumabweretsa mavuto ngakhale kwa anthu ena aphee. 215