Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 215

Miyambi ya Patsokwe Si mbewu yoisunga. -Mawuwa amanenedwa akamafotokoza za anthu ovuta kapena ana ovuta. Anthu ena akakwiya amanena mawuwa potanthauza kuti anthuwo ndi amphulupulu omwe sangawasunge pakhomo. Sikadza kokha kaopa kulaula. -Kuti munthu atukuke kapena apeze chimene akufuna amafu- nika kugwira ntchito mwakhama. Sikadza kokha, kaopa kulaula. -Ngati munthu akusowa chinthu ayenera kupita kukachifunafu- na chifukwa sichingamupeze pamene wakhalapo. Sikuli komire kwa apongozi. -Pachikamwini sipamafunika ulesi. Umafunika kugwira ntchito mwakhama m’malo modalira apongozi, chifukwa akatopa nawe akhoza kukuthamangitsa. Simbwesimbwe ananya chiwindi. -Munthu wochita zinthu kuti ena amutamande amadzakhaula tsiku lina. Sindinazione anachezera kuziona. -Pali zinthu zina zomwe zingakhala bwino kuti usakumane nazo kapena usayambe kuzichita chifukwa ukangoziyamba siziku- choka. Suku laliwisi silichedwa kukonyoka ndi mphepo. -Ana akakumana ndi mavuto samalimba. Zimene akumana nazo zikhoza kusokoneza tsogolo lawo lonse. Sunga khosi, mkanda woyera udzavala. -Munthu amafunika kupirira komanso kudziletsa kuti adzapeze zabwino m’tsogolo. 214