Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 214

Miyambi ya Patsokwe Saweruzika adamera nyanga pamphumi. -Nyama ina inauzidwa kuti kukagwa chilala nyanga zim- apangitsa kuti nyama izilephera kumwa madzi. Koma iyo sinamvere ndipo inameradi nyanga pachipumi. Chilala chi- tabwera inafa ndi ludzu chifukwa imati ikati imwe, nyanga zija zinkapezeka kuti zagunda pansi. Kumvera kumathandiza kuti tisakumane ndi mavuto oopsa. Saweruzika anamanga nyumba pamwala. -Munthu amene amadziyesa wodziwa zonse amalephera kufun- sa ena mapeto ake, amalakwitsa anthu n’kumuseka. Ndi bwino kumafunsa ena. Sayenda adabala mwana adayenda. -Usamachitire ena choyipa ngakhale iweyo suyenda chifukwa nthawi ina amadzayenda ndi mwana wako ndipo anthu una- wanyozawo amadzachitira choipa mwana wakoyo pobwezera zimene iwe unawachitira. Sayenda anabala mwana nayenda. -Tisamanyoze anthu amene amaoneka monyozeka chifukwa tsiku lina amadzachita zinthu zomwe sitimayembekezera. Sekerera cha nkhama, cha mano chiluma. -Zinthu zikamakuyendera, nthawi zina ndi bwino osasekerera (kusekerera cha nkhama) chifukwa ena akakuona sasangalala. Mwachitsanzo, kumangouza anthu kuti wagula wailesi kungachititse kuti akubere. Sekeserani, kumtondo kwanka ana, Sakhwi watsala yense. -Kusekesera ndi kusefa ufa. Munthu amanena mwambiwu aka- mauza mkazi wake kuti sanakhute, ndiye aphikenso chakudya china. 213