Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 21

Miyambi ya Patsokwe Bwato silidya. -Nsengwa, dengu kapena bwato zimangosunga zinthu zimene mwaikamo, sizimachepa kapena kuwonjezereka. Tizikhutira ndi zimene tili nazo pamoyo wathu. Bwenzi lako ndi la wina. -Tizichenjera ndi anzathu amene timacheza nawo chifukwa tika- wauza kathu, iwonso amakauza anzawo. Bwenzi mkoma uli moyo. -Pali anthu ena amene amakonda anzawo zinthu zikamayenda, koma zikavuta amawathawa. Bwenzi ndi mthanthira, mlamba udaolotsa khoswe. -Bwenzi lenileni liyenera kukhala lokonzeka kuthandiza mnzake akakumana ndi mavuto, osangoti pa zabwino zokha. Bwerera ali konse. -Mnzako akakuchitira chabwino umafunika kumuthokoza. Ko- ma iwenso umayenera kudzamuchitira zabwino, asamangochita yekha. Bza sapita kawiri. -Bza ndi mvekero wa kuthawa mwamwayi. Ngati munthu wap- ulumuka pa vuto mwamwayi, si bwino kubwereza kuchitanso zomwezo. 20