Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 209
Miyambi ya Patsokwe
Pawiripawiri sipauzirika.
-Munthu sungapemerere utsi ku mauna awiri a mbewa pa
nthawi imodzi. Munthu m’modzi sangachite zinthu ziwiri
nthawi imodzi zinthuzo n’kuyenda bwinobwino. Tizichita
chimodzi pa nthawi imodzi.
Payerepayere fisi anadya mkazi wake.
-Tsiku lina fisi anamva njala kwambiri ndipo anadya mkazi
wake. Anthu ena akasimidwa amangochita zinthu bola apu-
lumuke m’mavuto awo. Anthu oterowo amachita zinthu mwa
payerepayere ngati zimene fisi anachita podya mkazi wake njala
itavuta.
Pendapenda si kugwa koma kuchalira ulendo.
-Kulephera sikutanthauza kuti sungakwanitse kuchita chinthu.
Kuti munthu achite bwino amafunika kukumana kaye ndi
mavuto.
Phika mowa kuti umve amene anapha amako.
-Pamowa ndi pamene anthu amayankhula zakukhosi kwawo
ngakhale nkhani zachinsinsi. Munthu woledzera ndi mwana ndi
amene amanenadi zoona akafunsidwa zinthu. Kuti anthu aku-
uze zoona zenizeni umafunika kuwanyengerera monga ku-
wapatsa chinachake ndipo amasanza nkhani yonse.
Phiri siliyendera munthu.
-Munthu amene akufuna chinachake ayenera kupita kumene
chinthucho chimapezeka. Osamangodikira kuti chikupeza uli
pampando khale!
Phiri siliyendera nyani.
-Munthu amene akufuna chinachake ayenera kupita kumene
chinthucho chimapezeka. Osamangodikira kuti chikupeza uli
pampando khale!
208