Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 207

Miyambi ya Patsokwe limodzi zinthu zina monga kudyera limodzi mmemo. Tizigawana zinthu zimene tapeza limodzi. Papangano saika mwala. -Kumakwaniritsa malonjezo ako m’malo moikapo mwala. Papita mkazi mnzako, nawenso pitapo. -Nthawi zina ndi bwino kumachita zimene ena akuchita monga pamaliro ndi malo ena. Papita mnjere mpeni upita pomwepo. -Mnjere ndi chakunja cha zipatso ngati mandimu ndi malalanje. Munthu ukamasenda ndi mpeni, mpeniwo umangodutsa mom- we chikhungucho chathera. Munthu amalandira chilango malin- ga ndi zimene wapalamula. Nthawi zambiri munthuyo aka- kachita apilu, zimapezeka kuti mpeni umadutsa momwe wo- yamba uja unadutsa. Papsa tong’ola sudziwa mtima wa moto. -Ukamawotcha chimanga umafunika kumangodyeratu chifu- kwa ukapusa chimatha kupserera. Ndi bwino kumagwiritsa ntchito mwayi ukapezeka chifukwa zamawa sizidziwika. Pasamba mfulu, kapolonso amasambira pomwepo. -Munthu ukakhala pantchito, chomwe bwana wako wapeza monga phindu nawenso umadyerera nawo. Komanso ukakhala ndi anthu opeza bwino n’kumakhala nawo bwino umadyerera nawo. Pathindi Nkhwali, Mkango uli pomwepo. -Nkhwali ikati itere powirira nthawi zina pamakhalanso pali Mkango pomwepo. Pamene pali zabwino pamakhalanso mavuto. Ndi bwino kupirira mavutowo kuti upeze zabwinozo. Pati bii pali minga. -Pamene pali ntchire nthawi zambiri pamakhalanso minga. 206