Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 205
Miyambi ya Patsokwe
Palibe munthu amasula mfuti nkhondo itafika m’mudzi
mwake.
-Munthu uyenera kumakhala wokonzeka nthawi zonse kuti
udziteteze ku mavuto.
Palira mbirira pali khwawa.
-Pamene pakumveka madzi pamakhala kuti pali mtsinje kapena
khwawa. Mphekesera zikamamveka ndiye kuti chinachake
chachitika.
Pama loyesera limathyola chala.
-Munthu akalakwa pamafunika kumupatsa chilango chomuye-
nerera. Tikapereka chilango chankhanza timakhala tiku-
lakwiranso munthuyo.
Pamalima m’pamimba, khasu la Chidambo.
-Kuti munthu agwire ntchito amafunika kudya mokwanira.
Pamene wapsa supitapo kawiri.
-Pamene munthu wakumana ndi mavuto supitapo kawiri,
pokhapokha ngati uli woduka mutu.
Pamodzimodzi padawoletsa dzungu.
-Munthu amafunika kumayesanso zina. Osamangochita
chimodzimodzi chifukwa pamapeto pake sangatukuke.
Pamsasa saipitsa.
-Ukakhala pamalo achilendo umafunika kuonetsa khalidwe
labwino. Komanso ukachokapo si bwino kusiya utasokoneza
chifukwa umatha kukumana ndi mvula n’kufunanso utabw-
erera kunsasa komwe kuja.
Pamudzi pakakhala pa zitsilu, mkamwini asamakulirepo
mwendo.
-Si bwino kunyoza eni mudzi ngakhale akuoneka opusa, chifu-
kwa sudziwa zimene amapangana.
204