Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 203

Miyambi ya Patsokwe zoipa zomwe zimaoneka ngati zosangalatsa kumabweretsa mavuto oopsa. Osamakomedwa ndi zinthu. Pakadapanda Njiri kufera m’dambo, chizimba mukadayesan- ji? -Dzino la Njiri ndi mankhwala a khunyu komanso chizimba cha mankwala ena. Osamapsera mtima munthu amene watithandi- za, ndi bwino tizimuthokoza. Pakamwa ndi pa boma, ukasewera napo pakumangitsa. -Tiyenera kusamala ndi zomwe timanena chifukwa zikhoza kutiika m’mavuto. Pakamwa padzaulukira mbereswa. -Mawuwa amanena za munthu wina amene sanamvetse nkhani n’kumakauza ena. Anthu akamamudzudzula amamuuza kuti akamangoyankhulayankhula zomwe sanazimvetse, pakamwa pake padzaulukira mbereswa. Pakamwa pakudya zamchere. -Mawuwa amatanthauza kuti pakamwa pamatha kutuluka zabwino ndi zoipa zomwe. Munthu akhoza kulakwitsa ponena zinthu. Pakamwa palibe m’dima. -Munthu samaphonya pakamwa ngakhale akamadyera mumdi- ma, amakhala anapazolowera kwambiri. Munthu sangalephere kuchita zomwe anazolowera. Pakamwa pamawombola. -Anthu amene amadziwa kuyankhula amatha kupulumuka pa mlandu chifukwa chochenjera pakamwa. Pakamwa pamodzi sipalawa ndiwo. -Munthu m’modzi sanganene maganizo oimira anthu onse. Ti- mafunika kufufuza kwa enanso kuti titsimikizire. 202