Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 201

Miyambi ya Patsokwe Pachedwa msulu pali nyerere. -Kumene munthu amakonda kupita kapena chimene aku- chilimbikira ndiye kuti kuli chabwino chimene akuona kuti apezako. Pachoka mnzako pali malo. -Wina akasiya kuchita zinazake, anzake amapezerapo mpata wochita zinthuzo. Pachulu ndapaleka, ana a mbuzi angasewerepo. -Pachulu ndi pamene anthu amakonda kudzalapo ndiwo za- masamba chifukwa zimabereka bwino. Mawuwa amanenedwa munthu akasiya kuchita zinazake poopa kuti zingowonongeka. Pachulu palibe chiphe. -Anthu ena otchuka amakhala okoma mtima, koma pali ena osadziwika kwambiri omwe amakhala oipa mtima. Padiwa sasewera. -Tisamachite zinthu zomwe zikhoza kutiika m’mavuto. Padutsa khasu sipanama. -Kuchita khama pantchito kumabweretsa phindu. Mwachitsanzo, munthu amene wachita khama kulima sabwera chimanjamanja. Padyera mfulu, kapolo amadyera pomwepo. -Mnzako akakhala pabwino iwenso umadya nawo zimene amapeza. Padzikoli mpongoothera dzuwa, tikaothaotha timachokapo. -Moyo ndi waufupi, siuchedwa kutha. Umangokhala ngati una- badwa kuti udzaothere dzuwa kenako n’kuchokapo. Padziwa ndi pansi mwana wa mfuko akadwala. -Munthu wina akakuchitira chipongwe n’kuthawa, anthu amanena kuti, “Ingomulekani, akadzapezeka tidzaona naye 200