Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 20

Miyambi ya Patsokwe Bodza lilibe mwini. -Anthu amene sitimayembekezera kuti anganame nthawi zina amanena bodza m’maso muli gwa. Bodza limabwerera mwini wake. -Munthu ukanena bodza, bodzalo limakusakasaka mpaka ku- kupeza. Ndi bwino kumasamala ndi zimene timanena, ngati til- ibe nkhani ndi bwino kungokhala chete m’malo momapeka ma- bodza. Bololo sakonda madzi. -Pamene munthu watsimikiza kuchita kanthu kena, amakumana ndi mavuto komanso mayesero. Komabe, sayenera kulola kuti zimenezi zimulepheretse cholinga chake kapena kumugwetsa mphwayi. Bongololo anali ndiwo, timadya ndi a uje. -Si bwino kumadzitama pa zinthu zomwe sunapange chifukwa nthawi zina umangonama kuti unapanga. Bongololo sadzolera mafuta pagulu. -Si bwino kuulula zinsinsi zathu zonse, pali zinthu zina zomwe sitiyenera kuuza ena monga zam’banja. Nthawi zambiri munthu akaulula zimenezi amayalutsa banja lakelo. Bonongwe mkoma akadadza. -Nthawi zina mlendo amaonetsa makhalidwe abwino, koma akakhalitsa amaonetsa khalidwe lake lenileni. Buluzi kuthandiza mbewa kuthawa. -Nthawi zina anthu amene sitigwirizana nawo kapena amene sitiwadziwa ndi amene amatithandiza. Buluzi wa ize (mnyengo) anapanidwa ndi chitseko. -Kuchita zinthu zachinyengo monga chiwerewere kapena kuba kukhoza kutiika m’mavuto osaneneka. 19