Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 198
Miyambi ya Patsokwe
Osamafunsa za fungo m’chimbudzi.
-Mawuwa amanena za munthu amene akufunsa zinthu zoti aku-
zidziwa kale. Ndani angakhale pansi n’kumafunsa ngati ku-
chimbudzi kumanukha kapena ayi?
Osamagenda kupolisi chamba chili m’thumba.
-Kupalamula ukudziwa kuti uli ndi milandu ina.
Osamagulitsana makasu othyoka.
-Tisamachitirane zinthu zopanda chilungamo kapena kupusitsa
anzathu.
Osamaluma dzanja limene limakuthandiza.
-Osamanyoza kapena kuchitira chipongwe amene amakuthandi-
za.
Osamanyerera pambali pam’boo ukupaona.
-Osamachita zoipa, zabwino ukuzidziwa. Mwachitsanzo, ena
akakuuza malangizo oyenera oti uchitire zinazake iwe n’kuchita
zosiyana ndi zimenezo, umakhala ngati wanyerera pambali
pam’boo ukupaona.
Osamasambira molimbana ndi madzi, angakutenge.
-Si bwino kumachita zinthu zosiyana ndi zimene ena akuchita
chifukwa mapeto ake umatha kukumana ndi mavuto. Munthu
amene akusambira n’kumalimbana ndi madzi, amatopa ndipo
madziwo amamutenga.
Osamasewera paulimbo.
-Pali zinthu zina zomwe zikhoza kuwononga moyo wathu. Ndi
bwino kupewa zinthu zimenezo m’malo momachita masewera
n’kukumana ndi mavuto ngati mmene mbalame imachitira ika-
khala kuti imasewera ndi ulimbo.
Osamatsinira mafulufute kuuna.
-Osamachita zinthu zomwe zingatsekereze mwayi.
197