Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 195
Miyambi ya Patsokwe
Nyenderera zidatha kakule.
-Munthu akamachita zinazake mobisa, n’kupita kwa nthawi
amalephera kuzisiya.
Nyimbo imodzi sachezera gule.
-Kusinthasintha zinthu kumathandiza.
Nyundo m’masulano.
-Nyundo ndi hamala. Nyundo imathandiza kuti chigwandali
chikhale mpeni. Ndi bwino kumathandizana.
Nyumba imayamba ndi njerwa imodzi.
-Zinthu zikuluzikulu zimayamba ndi zing’onozing’ono.
Nyumba ya chitsiru siipsa.
-Nthawi zina pooneka ngati wopusa, umapewa mavuto ambiri.
Nyumba ya mwini saotchera mbewa.
-Munthu wina ankatenthetsa madzi oti akawaze m’nyumba kuti
aphe mphutsi. Mlendo wake ankaganiza kuti akuphika msima
moti anaotcha mbewa zake. Anadikirira koma nsima sinabwere.
Osamadalira zinthu za ena tikamachita zinthu monga kukwatira
tikuganiza kuti makolo adzatithandiza.
Nyumba yabwino imakhala ndi moto.
-M’nyumba kuti mukhale mosangalatsa muyenera kukhala zin-
thu zofunika monga zakudya.
Nzeru ndi chuma.
-Munthu wanzeru ndi amene amatukuka komanso kukhala
moyo wabwino.
Nzeruzayekha adaviika nsima m’madzi.
-Ngati tikukayika kapena sitikudziwa zoyenera kuchita ndi
bwino kufunsa kuti tichite zinthu moyenera.
194