Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 193

Miyambi ya Patsokwe Ntchenzi idamva mawu oyamba. -Munthu wina ananena kuti, “Nditchera msampha mawa,” ke- nako anasintha n’kunena kuti lero. Ntchenzi inangomva mawu oyambawo ndipo inabwera n’kugwidwa. Tizichenjera tikamanena zinthu chifukwa anthu amagwira mawu anthu oyamba. Ntchenzi m’mbuyo. -Mawuwa amanena za munthu wabodza. Anthu amanena mawuwa pofuna kuchenjeza anzawo kuti achenjere, wama- bodza akubwera. Ntchito ndi mumtengo. -Munthu ukakhala pantchito uyenera kukhala mosamala ngati mmene umachitira ukakwera mumtengo chifukwa nthawi ili- yonse ikhoza kutha, ukhoza kutsakamuka. Ntchito siichepa. -Ntchito ingakhale yonyozeka tiyenera kuigwira mosamala ko- manso mwakhama. Ntchito zimatsata msinkhu. -Munthu wamkulu sayenera kumachita zibwana. Nthawi siidikira munthu. -Kaya ukutani, nthawi simayembekezera kuti uchite kaye zim- enezo, imangopitabe. Nthunzi sufuka pachabe. -Nkhani simangomveka, pamakhala kuti pachitika chinachake. Nyalugwe m’chepsa chamnzake, iye akapha chiwala achita ku- koka. -Pali anthu ena okonda kunyoza za anzawo koma amakometsa zawo ngakhale zitakhala zosalongosoka. 192