Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 192

Miyambi ya Patsokwe chifukwa cha khalidwe lake loipa. Nsomba ikaola imodzi, zaola zonse. -Pamudzi munthu akakhala wamakhalidwe oipa monga waku- ba, anthu amangoti mudzi wonse ndi wa anthu akuba ngakhale wakuba ali m’modzi yekha. Kulakwa kwa munthu wina kukho- za kukhudza anthu ena. Nsomba ndi therere saphika mphika umodzi. -Nkhani kapena zinthu zosiyana si bwino kuzikambira pamodzi. Chilichonse chiyenera kuonedwa pachokha. Nsungwi yantuwa sisiriridwa. -Nsungwi yantuwa ndi yosakhwima. Palibe munthu amene an- gaidule kuti akachitire chinachake chifukwa imakhala yosalim- ba. Munthu akakhala waulesi amuna kapena akazi samufuna. Munthu azionetsa chamuna. Nsupa ndi nsupa, mulibe thonje. -Munthu amadziwika ndi khalidwe lake. N’zoona kuti tonse ndi anthu, koma timasiyanabe zochita. Makhalidwe abwino azionekera poyera. Ntchembere yamapasa izigona chagada. -Ukakhala pakati umaona mbali zonse ziwiri n’kumapereka thandiza kumene kukufunikira. Ntchentche inati, “m’tsogolo moyo, m’mbuyo moyo.” -Si bwino kumachoka pamalo utaipitsapo chifukwa tsiku lina udzafunanso kubwererapo. Ntchentche yadyera inapita ndi maliro kumanda. -Munthu wotengeka ndi zilizonse amataika n’kukumana ndi mavuto. Ntchentche yojijirika inaphinjidwa ndi nchimba. -Si bwino kukhala anthu ojijirika, tingakumane ndi mavuto. 191