Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 191

Miyambi ya Patsokwe Nsapato imodzi savala anthu awiri. -Anthu angapo sangakhale pa udindo umodzi. Nsengwa siidya. -Nsengwa, dengu kapena bwato zimangosunga zinthu zimene mwaikamo, sizimachepa kapena kuwonjezereka. Tizikhutira ndi zimene tili nazo pamoyo wathu. Nsengwa ya muyeso amathyola ndi anansi. -Nthawi zina anthu amene amakhala adani athu chifukwa chowononga zinthu zathu amakhala achibale kapena ena apa- fupi. Nsengwa ya nsima savundikira ndi chikho. -Timafunika kusamala zinthu zathu pozisunga pabwino kuti zisawonongeke. Nsengwa yobwereka samangira banja. -Kuti munthu akwatire kapena achite zinazake amafunika ku- konzekera m’malo momadalira zinthu za ena. Nsikidzi zikalumaluma zimalowa m’tsekera. -Mawuwa amanena za anthu omwe amati anzawo akawachitira zabwino amangozimiririka osathokoza. Nsikidzi zinachilira kwa alendo. -M’nyumba anthu akhoza kukangana koma kukabwera alendo anawaonetsa chikondi komanso amaoneka ngati ogwirizana ndipo nthawi zina mkanganowo umathera pomwepo. Nsima ya apongozi sasungira mlendo, ngakhale yochokera kwa apongozi. -Apongozi monga makolo, umayenera kuwapatsa ulemu waukulu. Nsomba ikawola imodzi, zonse zawola. -Munthu m’modzi wosokoneza amaipitsa mbiri ya anthu ambiri 190