Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 190

Miyambi ya Patsokwe Nsabwe yoyendayenda inakumana ndi chala. -Munthu woyendayenda salephera kupalamula. Nsalu ndi kukhosi. -Aliyense ali ndi ufulu wosankha chimene chamukomera kapena chimene akufuna kuchita. Nsalu ya “lekaleka.” -Mawuwa amatanthauza mwana. Nthawi zambiri ana ama- konda kugwiragwira ndipo mayi awo angamawaletse kuti aleke. Akakhala wakhanda, mayi salola kuti aliyense amunya- mule poopa kumukhonyola. Amauza munthuyo kuti aleke. Nsalu yobwereka silimba m’chiuno. -Zinthu zobwereka zimakhala zosadalirika, choncho ndi bwino kumasamala chimene wabwereka kuti ukachibweze chili bwino. Nsalu yobwereka sithetsa usiwa. -Kubwereka zinthu kwa ena si njira yothetsera umphawi koma kugwira ntchito kuti tipeze zimene tikufuna. Nsangala za pamaliro ngati matenda adakazonda. -Kujijirika pa zinthu zoti wapeza zothaitha kapena zochitidwa kale, pomwe poyamba unalibe nazo chidwi. Nsanjikizo udaphetsa Kunda. -Kunda ndi mbewa. Kunda ankasunga zinthu zambiri zomwe tizilombo tina timafuna kudya nawo. Kunda anayamba kulim- bana ndi tizilomboto mpaka anaphedwa. Tizipewa kuchita zin- thu zomwe zingatibweretsere mavuto. Dyera si labwino, lima- bweretsa mavuto. Nsanza zili ndi ntchito. -Si bwino kumawononga zinthu zakale monga chikhalidwe cha makolo chifukwa chimakhalabe ndi ntchito. 189