Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 188

Miyambi ya Patsokwe Nkhuku imalemekezeka ndi nthenga zake. -Munthu amalemekezeka chifukwa cha khalidwe komanso zo- chita zake. Nkhuku yanjiru simaswa mazira. -Nsanje simapindulitsa munthu. Umafunika kulimbikira ntchito m’malo momangokhalira kulimbana ndi anzako omwe ziku- wayendera. Nkhuku yoweta sagula pamsika. -Mkazi wabwino samakapena koyenda. Nkhululu yatcheru ndiyo imaimba lokoma pachilimwe. -Pa nthawi ya dzinja, Nkhululu imatolera zakudya n’kukasiya kuuna ndipo simadzavutika m’chilimwe. Tizichita zinthu zom- we zidzatithandize m’tsogolo. Nkhuni imodzi siipanga mtolo. -Munthu payekha sangakhale ndi nzeru zonse, umafunika kumva maganizo a ena. Nkhuni imodzi siipsetsa mphika wa nyemba. -Munthu payekha sangakhale ndi nzeru zonse, umafunika kumva maganizo a ena komanso kulola kuti akuthandize. Nkhunzi yamwini sang’ambira khola. -Munthu sangakulitse khola lake chifukwa cha tonde kapena ng’ombe yamwini. Tizidalira zanthu osati za eni. Nkhunzi yobwereka samangira khola. -Si bwino kudalira chinthu chobwereka chifukwa mwini wake akhoza kuchifuna nthawi iliyonse. Nkhutukumve. -Mawuwa amatanthauza munthu wosamva, amene amangochi- ta zake. 187