Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 187

Miyambi ya Patsokwe Nkhani ndi kamnyamata. -Kucheza sikutha, nkhani zikayamba zimabwerabe zina. Ndi bwino kumaona polekezera kucheza kuti tizigwira ntchito. Nkhani siidzala mtanga. -Kucheza sikutha, nkhani zikayamba zimabwerabe zina. Ndi bwino kumaona polekezera kucheza kuti tizigwira ntchito. Nkhani siikalamba. -Kucheza sikutha, nkhani zikayamba zimabwerabe zina. Ndi bwino kumaona polekezera kucheza kuti tizigwira ntchito. Nkhani yalowa m’chala. -Anthu ena amapondereza nkhani chifukwa choti wolakwayo ndi m’bale wawo kapena wawapatsa chiphuphu. Zikatere timati nkhaniyo yalowa m’chala. Nkhokwe imalimba ndi mphanda. -Munthu aliyense amafuna wina woti azimuthandiza. Kudali- rana n’kofunika. Nkhondo kadzikumbire. -Nthawi zina pofuna kupezetsa ena mavuto, timapezeka kuti ta- wavala mavutowo n’kukhaula nawo. Kutchera msampha kuti wina akodwe, n’kupezeka wakodwa wekha. Nkhondo ndi anansi -Amakuchitira choipa nthawi zina ndi abale ako kapena amene umakhala nawo pafupi. Nkhonya ya “mudandiyambakale” idagwa m’chikope. -Mkwiyo ndi woopsa. Kusunga chidani kumachititsa kuti mun- thu uchite zoopsa kwambiri. Nkhope ya muthu imanola khope inzake. -Munthu amathandiza mnzake kuti azichita bwino. 186