Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 186

Miyambi ya Patsokwe Njuchi zikachuluka siziika. -Anthu akachuluka pamalo kapena pantchito, zinthu siziyenda. Aliyense amangosiira mnzake. Njuchi zikachuluka zilibe usinda. -Anthu akachuluka pamalo kapena pantchito, zinthu siziyenda. Aliyense amangosiira mnzake. Njuchi zingalume, koma ine phula nditenga. -Kuti upeze zabwino umafunika kulimba mtima komanso kupirira mavuto. Kuti munthu afule njuchi n’kutenga malesa, njuchi zina zimamuluma koma iye sagonja mpaka atatenga uchiwo. Nkhali imafuna mafuwa. -Aliyense amafuna wina woti amuthandize. Nkhali yodikirira imachedwa kuwira. -Chilichonse chili ndi nthawi yake, ndi bwino kumadikira. M’malo mongokhala ndi bwino kumachita zina kuti usaone kuchedwa. Nkhanga ikakula, siikhala paphira. -Munthu ukakula umayenera kusiya chibwana. Nkhanga yaikulu saweta. -N’zovuta kusintha Nkhanga yaikulu kuti ikhale yoweta. Mun- thu amene wakula ndi zizolowezi zoipa amavuta kumusintha. Nkhanga zinapangana kusanaspe. -Ndi bwino kumaganizira zimene tingachite mavuto atatigwera, kusiyana n’kumakhala pansi kuti tidziwe chochita mavutowo akatipanikiza. Nkhani ndi kamchira, umafunika uyang’ane kaye pali mutu wake. -Kumafufuza chimene chachititsa vuto. 185