Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 185

Miyambi ya Patsokwe Njira salimbira, chikakula patuka. -Pali zinthu zina zomwe sitingalimbane nazo, zoterozo zimafuna kungozisiya. Njira ya kwa amfumu siiwirira. -Nkhani zonse zofunika kwambiri kaya ndi za maliro, zima- yenera kukanenedwa kwa amfumu kuti akuthandizeni. Njira zonse sizipita pamutu pako. -Nthawi zina ndi bwino kulola kuti zinthu zina zitipite. Njiwa sasosolera pamsampha. -Ukasosolera njira pamsampha, zinzake zimadziwa, n’kuchenje- ra. Tisamaulule zinthu zomwe tikudziwa kuti zikhoza kupereka mphamvu kwa ena kuti atilange. Njoka ndi njoka, singasinthe manga. -Munthu woipa ndi woipa, sangasinthe ngakhale mutamulangi- za bwanji. Njoka yopusa imalumira kumchira. -Pali anthu ena ooneka opusa, anthuwa sitimadziwa zimene akuganiza kusiyana ndi ena omwe akungolongolola. Njovu idagwa m’mbuna mwa Aonenji. -Munthu aliyense ali ndi mwayi wake. Choncho, si bwino ku- ganiza kuti anthu ena ooneka onyozeka sangapeze mwayi. Njovu inatuma nyerere. -Mawu onena moseka omwe ena amagwiritsa ntchito ak- amatuma mwana kapena munthu wonyozeka. Njuchi yako ndi iyo yaluma. -Osamangotsata zinthu zomwe ulibe nazo umboni. Kumatsata zinthu zenizeni. 184