Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 182

Miyambi ya Patsokwe kutchukako sikuchedwa kutha. Zikamakuyendera bwino kwam- biri dziwa kuti zikhoza kukusokonekera. Ng’ombe ya mnzako sumaiitana. -Tisamale ndi zinthu za ena kuti nawonso asamale zinthu zathu. Ng’ombe yaukali imagwa m’mbuna. -Munthu ukakhala waukali, anthu samakuchenjeza ngati pena pali zoopsa chifukwa amaopa kuti uwakalipira. Munthu wofatsa ndi amene amathandizidwa ndi ena. Ngakhale chitsiru nachonso chili ndi amake. -Aliyense anganyanse bwanji, angaipe bwanji, amakhala ndi abale ake komanso anthu amene amamukonda. Ngakhale matako atafunitsitsa bwanji, sangakhale kutsogolo. -Pali zinthu zina zomwe sitingakwanitse kuchita ngakhale titafu- nitsitsa bwanji. Ngakhale nkhalango ikamapsa, Birimankhwe sasintha mapondedwe. -N’zovuta kusintha zimene unazolowera. Ngakhale wapamtima, usamuuze mawu onse akukhosi. -Mnzako amene umamukhulupirira amakhalanso ndi anzake moti chinsinsi chimene wamuuza amakauzanso anzakewo nkhaniyo n’kufala. Ngaluwe idalira msampha utaning’a. -Mawuwa amanena za kulephera kupirira vuto litatsala pang’ono kutha. Ngati mtengo wauwisi ukuyaka, ndiye wouma ungatani? -Mawuwa amanenedwa ngati munthu wolimba kapena amene amachita bwino zinazake walephera. Ngati zotere zitachitika ndiye kuti ena omwe si olimba amangogweratu. Zimene zavuta 181