Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 181
Miyambi ya Patsokwe
kuchita zinazake n’kutaya mphamvu zake pachabe.
Ndiwonetsetse adathetsa nkhosa.
-Kuzengereza pochita zinthu kumapezetsa mavuto.
Ndodo imodzi siipha njoka.
-Mawuwa amanenedwa pofuna kulangiza ena kuti afunika ku-
machita zinthu mobwereza osati kamodzi kokha.
Ndodo ya ana ndi imene amaphera njoka.
-Osamanyoza maganizo a ana. Nthawi zina mnzeru zawo ndi
zimene zimathandiza pamavuto, monga njoka ikalowa m’nyum-
ba umatha kutenga ndodo yomwe mwana amaseweretsa
n’kuphera njoka.
Nena chilungamo n’kuthawa.
-Nthawi zina munthu ukanena chilungamo anthu amakuda. Ko-
ma kunena chilungamo n’kofunika. Choncho, zimakhala bwino
kunena chilungamo koma umafunika kusamala chifukwa ukho-
za kukumana ndi mavuto.
Nena poipa kuti pabwino patuluke.
-Munthu ukamafuna kudzudzula choipa umanena ngati nthab-
wala kuti nkhaninkhani ituluke n’kukonzedwa.
Ng’oma imalira ikaona inzake.
-Anthufe timafunikira anthu ena kuti zinthu zitiyendere bwino.
Mwachitsanzo, kuti munthu usangalale ndi phwando umafu-
nika anzako.
Ng’oma silira yokha.
-Ng’oma ikamalira ndiye kuti wina akuimenya. Chimodzimodzi
munthu, akamadandaula pakakhala kuti penapake pali vuto.
Ng’oma yolira bwino sichedwa kung’ambika.
-Munthu ukatchuka kwambiri usamadzitame chifukwa
180