Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 180

Miyambi ya Patsokwe Ndi mwamuna akadya. -Munthu ayenera kuonetsa chamuna chake pogwira ntchito osati pakudya pokha. Ndi mwamuna pakudya pokha. -Munthu ayenera kuonetsa chamuna chake pogwira ntchito osati pakudya pokha. Ndikanadziwa ndikanaphika therere. -Mkazi wina ankayembekezera kuti mwamuna wake abweretsa nyama kuchokera ku uzimba. Koma anadandaula mwamuna wake atabwerako chimanjamanja. Mawuwa amanenedwa zinthu zimene umayembekezera zikakhala kuti sizinachitike, ndiye ukudandaula kuti bola ukanachita zinthu zina. Ndikhale nawo analanda malo. -Si bwino kumangolola anthu osadziwika bwino kuti mukhale nawo pamudzi kapena kuwapatsa udindo chifukwa pamapeto pake amakhala eni mudzi. Tizisamala ndi anthu omwe sitiku- wadziwa bwino. Ndikudula tsitsi ndi mano. -Mawuwa munthu amawanena akakhala kuti wavutika kapena wasauka kwambiri. Ndim’khulupirira adam’gonetsa m’nkhufi. -Munthu amene umamudalira, nthawi zina ndi amene amaku- khumudwitsa kwambiri. Ndimveke ndine adaphetsa fisi. -Kususukira kutchuka kumabweretsa tsoka. Ndinatha Ngombo ndi Akamundi, kuli Achanga ndisanafike. -Munthu amanena mawuwa podandaula kuti akanadziwa kuti zabwino zili kutsogolo akanadikira. Amakhala kuti anafulumira 179