Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 178
Miyambi ya Patsokwe
chifukwa choti anthu sanamumvetse bwino.
Ndabwerera pakamwa pa Mkango.
-Mawuwa amenena za munthu amene wapulumuka pamavuto
aakulu.
Ndagunda, dziko lonse landimva.
-Mawuwa amanena za munthu amene watchuka padziko lonse
chifukwa cha ntchito zake.
Ndakutama kukongola kwako, nzeru zako sindizitama.
-Mawuwa amatanthauza kuti, ngakhale munthuyo ali wokongo-
la koma ndi wamakhalidwe oipa.
Ndakwatiwa kumbuyo, kumaso kulira ena.
-Mawuwa amanena za munthu amene wakwatiwa ndi munthu
wolemera koma mwamuna wake ndi gojo, sangathe kumupatsa
ana.
Ndakwatiwa n’kumbuyo komwe.
-Wakwatiwa ndi munthu wabwino, wachuma komanso wakha-
lidwe labwino.
Ndalama zidaphetsa Yesu.
-Anthu ena amachita zolakwa zikuluzikulu chifukwa chokonda
ndalama.
Ndalama zikamayankhula, chilungamo chimakhala chete.
-Nthawi zambiri anthu ena amatha kupereka ziphuphu kuti
mlandu wawo uyende bwino. Zimenezi zimachititsa kuti osala-
kwa amangidwe kapena chilungamo chisaoneke.
Ndalowa m’chala.
-Mawuwa amatanthauza kudwaladwala. Anganenenso za mun-
thu yemwe anali wachuma koma anasauka, moti akusowa pog-
wira.
177