Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 176

Miyambi ya Patsokwe Mwezi satungira mkanda. -Ntchito iliyonse ili ndi nthawi yake yoyenera kugwiridwa. Ku- chita chinthu pa nthawi yolakwika sikuthandiza. Mwachitsanzo, kufuna kulowetsa ulusi pabowo la singano usiku pa kuwala kwa mwezi. Mwezi sayanikira ufa. -Pali zinthu zina zomwe zimachitika masana okha kapena pa nthawi yake osati nthawi iliyonse. Mwezi uli kumwamba, mitengo ili pansi. -Pali zinthu zina zomwe zili kutali zomwe n’zobisika kwa anthu koma zina n’zodziwika kwa aliyense ngati mitengo yomwe ili pansi pano. Mwini phala sada chala. -Nthawi zambiri munthu saona kulakwa kwake kapena kwa ana ake. Mwiniwake wapha pa mbewu yake. -Mawuma amanena za munthu yemwe amapha anthu a pabanja pake kuti achitire zizimba. Zimenezi ndi zina mwa zimene an- thu a ku Africa kuno amakhulupirira zomwe zilibe umboni kuti zimathandizadi. Myang’ana dzuwa adasochera. -Munthu amene safunsa nthawi zambiri amakumana ndi mavuto ngati mmene zimakhalira ndi munthu amene amayan- g’ana kumene kuli dzuwa akamayenda ulendo. Dzuwalo li- masuntha ndiye amasokonekera n’kusochera. Myendera mwana salema. -Munthu akakhala ndi mwana wake satopa kumuyendera. Tikamachita chinthu sitiyenera kutopa mpaka titachikwaniritsa. 175