Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 175

Miyambi ya Patsokwe Mwayi ndi mwayi. -Ngati munthu wapeza mwayi wochita zinazake ndi mwayi wake basi. Mwayi sudziwika. -Tizingochita zomwe tikuganiza kuti zingatithandize. Mwayi sufanana. -Anthufe timapeza zinthu mosiyana. Mwayi sulingana. -Anthufe timapeza zinthu mosiyana. Mwayi wa mnzako sagonera pabwalo. -Si bwino kungochita zinthu chifukwa choti waona kuti wina zamuyendera bwino. Mwachitsanzo, chifukwa choti wina wachita chinachake n’kuyenda bwino, si ndiye kuti iwe ukachi- tanso zomwezo zikuthera bwino. Mwayi wa munthu mmodzi sangagonere wina pabwalo. -Mwayi umasiyana. Tisamachite zinthu chifukwa choti anzathu atachita zomwezo zinawayenera bwino. Mwayi wamzama wofukula ndi manja. -Mwayi waukulu kwambiri. Mwazi ukutuluka pampini. -Mawu otanthauza kuti pakuchitika zodabwitsa. Mwendo wa amfumu kulemera. -Anduna akampempha anthu kuti atumidwa ndi amfumu kuti apemphe thandizo lawo anthuwo n’kukana ndunazo zimamva mwendo wa mfumu kulemera. M’mawu ena zimaona kuti udindo wawowo ndi wolemera kwambiri. Mweranitu, ukadza kuno subwerera, ndigubula. -Mwayi kapena nthawi ikapezeka, ndi bwino kuchitiratu chifu- kwa zamawa sizidziwika. 174