Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 174

Miyambi ya Patsokwe zinthu zambiri zomwe zingachititse kuti azipitapita ku- chimbudzi. Mwana yemwe amasamba m’manja amadya ndi akuluakulu. -Munthu amene ali ndi khalidwe labwino kapena wolimbikira ntchito amakondedwa ndi ena ndipo zinthu zimamuyendera bwino. Mwandimangitsa madzi m’masamba. -N’zosatheka kumanga madzi m’masamba. Choncho mawuwa amatanthauza kuti mwandipusitsa. Mwandimangitsa madzi m’mayani. -N’zosatheka kumanga madzi m’masamba. Choncho mawuwa amatanthauza kuti mwandipusitsa. Mwandiyesa “kankhuku kadza ndi yani?” -Mawu otanthauza kuti mukuyesa ndine mlendo? Mwandiyesa kankhuku kachilendo. -Mawu otanthauza kuti mukuyesa ndine mlendo? Mwaupaka matope, mpanje wakanika kulira. -Ng’oma ikakhala ndi matope siimveka bwino. Tizionetsetsa kuti zonse zili bwino tisanayambe kuchita zinthu. Mwauza Kambuku kugwira pakhosi. -Ngati Kambuku wagwira nyama pakhosi ndi kuti yapita imen- eyo. Chimodzimodzinso kulekerera anthu kuchita khalidwe loipa kumakhala ngati kulimbikitsa khalidwelo. Mwavomera chamutu, mtima wakana. -Mawu otanthauza kuti simunavomere ndi mtima wonse. Mwayi kusiyana. -Anthufe timapeza zinthu mosiyana. 173