Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 173

Miyambi ya Patsokwe a Ng’azi. Mwana wa Ng’ona sakulira dziwe limodzi. -Mwamuna sakulira malo amodzi. Amafunika kuyendayenda kuti akasake ndalama zothandizira mkazi komanso abale ake. Mwana wa Ng’ona salephera kuyangalala. -Nthawi zambiri ana amatengera luso la makolo awo. Ng’ona imayendayenda m’madzi chifukwa ndi zimene makolo awo amachita. Mwanapiye kunyera m’nyumba awonera mayi ake. -Zimene makolo amachita ndi zimene ana amatengera. Mwana wa Nkhuku chenjera, Kabawi watulukira. -Mawuwa amakonda kunena ndi ogwira ntchito akamachenjeza anzawo kuti abwana kapena owayang’anira akubwera. Mwana wa pang’oma salephera kuyangala. -Nthawi zambiri mwana amatengera khalidwe la makolo ake. Mwana waulemu amakodza kwambiri. -Munthu waulemu amapeza zinthu zambiri pakati pa anzake. M’mawu ena amadya zambiri zomwe zimachititsa kuti az- ingokodzakodza. Mwana wokhulupirika amakodza pogona. -Mwambiwu amaunena akamalimbikitsa mwana kapena mun- thu wina kuti akakhala wotumika kapena wokhulupirika anthu azimupatsa zinthu zambiri zomwe zingachititse kuti azikodza pogona chifukwa chokhuta. Mwana wokhulupirika amanyera nchimba waukulu. -Mwambiwu ndi woumitsa pakamwa, koma ena amaunena momasuka akamalimbikitsa mwana kapena munthu wina kuti akakhala wotumika kapena wokhulupirika anthu azimupatsa 172