Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 167
Miyambi ya Patsokwe
Mutu umodzi susenza denga.
-Palibe munthu amene angathe kuchita zonse payekha. Chon-
cho, ndi bwino kumadalirana komanso kuthandizana.
Mutu wodwala Kasire adatema Kadzidzi.
-Zochita za ena zimatha kubweretsera ena mavuto. Si bwino ku-
lola kupusitsika ndi maonekedwe.
Muvi kalase Nungu.
-Munthu ankafuna kulasa Nungu ndipo Nungu inamulasa ndi
minga yake. Nthawi zina choipa chimene munthu akufuna ku-
chitira mnzake chimatha kumutembenukira.
Muvi woyang’anira suchedwa kugwera m’maso.
-Mavuto owayang’anira amakula kwambiri, monga matenda.
Tisamadikire kuti zinthu zifike poipa. Komanso, kuzengereza
kumagwetsera munthu m’mavuto.
Muvi woyang’anira suchedwa kulowa m’maso.
-Mavuto owayang’anira amakula kwambiri, monga matenda.
Tisamadikire kuti zinthu zifike poipa. Komanso, kuzengereza
kumagwetsera munthu m’mavuto.
Mvera uphungu ndipo utsatire malangizo kuti udzakhale
wanzeru m’tsogolo.
-Kumvera malangizo kumanthandiza kuti munthu apewe
mavuto.
Mvula ikakuona litsiro sikata.
-Nthawi zina mavuto akakuyamba sakusiya.
Mvula ya mpoto kunyenga mkamwini.
-Si bwino kutengeka ndi zinthu zomwe zimaoneka ngati si zoipa
kwenikweni chifukwa pamapeto pake zimachititsa kuti tidziim-
be mlandu kapena tikumane ndi mavuto.
166